National News

KWATHA! CHAKWERA WATHETSA MILANDU YA CHIZUMA

President Lazarus Chakwera walamula kuti milandu yonse yomwe mkulu wa bungwe la ACB, Martha Chizuma akuzengedwa ithe.

Mkulu ozenga milandu ya boma, Masauko Chamkakala watsimikiza izi ndipo wati walankhula kale ndi magulu onse okhudzidwa kuphatikizapo ofesi ya mlangizi wa boma paza malamulo.

A Chizuma amayankha mulandu olingana ndi zomwe adalankhulana ndi a Anderson Mwakyeru pa lamya zokhudza ofesi yawo.

KWATHA! CHAKWERA WATHETSA MILANDU YA CHIZUMA

Izi zikudza patapita masiku ochepa boma litapeza maloya awiri apadera kuti athandizire pa nkhani-yi maka kutsutsa ganizo loti a Chizuma asaime pa ntchito.

 

Dziko la America lidanenetsa kuti boma la Malawi likapitilira kuzunza a Chizuma lipereka zilango zina kudziko lino ponena kuti utsogoleri wa dziko sukuwonetsa chidwi cholimbana ndi katangale.

265 Magazine

265 Magazine is an online publication run by Malawian journalist with the core purpose of bringing most reliable news to the population.
Back to top button
Close
Close

Adblock Detected

Please disable ad blocker for this website so we continue giving you best news.